Dziko Lonse Likulira: Papa Francis Wamwalira
Football Association of Malawi (FAM) yalengeza kuti yatsata mozama zomwe zikunenedwa zokhudza kuchitidwa zachiwerewere kwa membala wa gulu la amayi la mpira wa miyendo ku Malawi (The Scorchers) panthawi ya ulendo waku South Africa.
![]() |
| Malawi women's football team |
Malinga ndi kalata yovomerezeka yotulutsidwa ndi FAM, bungweli layamba kafukufuku kuti likapeze zoona pa nkhaniyi. FAM yatsimikiza kuti njira zonse zotsatira kafukufukuyu zizikhala motsatira malamulo ndi ndondomeko zake zomwe zimatsimikizira chilungamo komanso ufulu wa aliyense yemwe akukhudzidwa.
FAM yawonetseranso kudzipereka kwawo pa chitetezo, ulemu, ndi thanzi la osewera komanso akuluakulu onse m’gulu la mpira, potsatira malamulo awo a safeguarding policy.
Bungweli latsimikiza kuti lidzapitiriza kupereka zambiri pamene akuchita kafukufukuyu.
Tikuyembekezera zochitika za m’tsogolo, koma chofunika kwambiri ndikuteteza ufulu wa amayi komanso kuonetsetsa kuti mpira wa miyendo ukuchitika m’njira yowona mtima komanso yolemekeza aliyense.
#TransformingTheGame
#FAM #TheScorchers
Comments
Post a Comment