Dziko Lonse Likulira: Papa Francis Wamwalira
Usiku wa dzulo, ngozi yochititsa mantha idachitika pa madzi a Nyanja ya Malawi m'chigawo cha Likoma, pomwe sitima yaying'ono idamira, n’kupha anthu atatu pomwe ena asanu ndi atatu apulumutsidwa.
Malinga ndi mneneri wa apolisi ku Likoma, Sergeant Enala Kalua, ngoziyi idachitika pamene anthu ankayenda mu bwato laling'ono kuchokera kumtunda kufuna kukwera sitima ya Chilembwe yomwe inali pakati pa nyanja, ikuchoka ku Mangochi kupita ku Nkhata Bay.
Kalua adati, bwato laling’onolo lidamira ndi anthu onsewo ali m'njira yopita kukakwera sitimayo. Panopa apolisi limodzi ndi ogwira ntchito yadzidzidzi akupitiriza kufufuza kuti adziwe chiwerengero chenicheni cha anthu amene anali m'bwatomo komanso amene akusowa mpaka pano.
“Ili ndi tsoka lalikulu, ndipo tikupempha anthu kukhala tcheru akamayenda pa madzi, makamaka pa nyengo ya mphepo kapena madzulo,” Kalua adatero.
Tikutumiza mawu achisoni kwa mabanja a onse omwe ataya okondedwa awo chifukwa cha ngoziyi.
Comments
Post a Comment