Dziko Lonse Likulira: Papa Francis Wamwalira

Image
Lero dziko lonse likulirira. Mtumiki wathu, mtumwi wa mtendere, mtsogoleri wa Tchalitchi cha Katolika Papa Francis   wamwalira ali ndi zaka 88 . Nkhaniyi yatsimikizidwa ndi Vatican m'mawa uno, ndipo ikufalikira mofulumira padziko lonse lapansi. Papa Francis  Papa Francis, anabadwa ngati Jorge Mario Bergoglio ku Argentina, anali Papa woyamba kuchokera ku America, komanso wa mtundu wa Jesuit. Kuyambira atasankhidwa mu March 2013 , anasankha dzina Francis osati chifukwa chokopa, koma kuti akhale ngati Mtumiki wa osauka St. Francis of Assisi . Sanali Papa wa mphamvu anali Papa wa mtima . Anakana kukhala m'nyumba zokongola za Vatican, ndipo anasankha kukhala m'chipinda chaching'ono chisonyezo cha moyo wake wopanda kudzikuza. Papa Francis anali wolimba mtima. Anayankhula za kusintha kwa nyengo (climate change), kusasiyana kwa olemera ndi osauka, kulandira othawa kwawo, komanso za chikondi cha Mulungu kwa aliyense – ngakhale amene ena amawawona ngati osayenera. Anati: “...

Zinyalala Zachuluka ku Msika wa Chinamwali: Amalonda Ayamba Kulankhula Mokweza Mawu

 


Msika wa Chinamwali mu mzinda wa Zomba wasanduka ngati malo osiyira zinyalala. Kwa mwezi wathunthu tsopano, khonsolo ya mzindawu sinachotse zinyalala zomwe zikungokulirakulira tsiku ndi tsiku.



Malinga ndi Kanfosi Jalisi, m'modzi mwa amalonda omwe amagulitsa ku msikawu, vutoli layamba kuwonetsa kuti litha kubweretsa matenda chifukwa cha kusowa ukhondo. "Zinyalala zikuchuluka, ndipo tilibe chitetezo chaumoyo. Anthu amatha kudwala ndipo ife amalonda timavutika kugwira ntchito m'malo osachita bwino atero," anatero Jalisi, amene sanabisenso kukhumudwa kwake.

Iye anafotokozanso kuti amalonda a m'msika wa Chinamwali opitilira 1,500 alankhula kuti akagwiritsa ntchito ndalama zawo zokha kuchotsa zinyalala ngati khonsoloyi sipereka chithandizo. "Timapereka ndalama zambiri pa tsiku, koma sitikuona ntchito yeniyeni yachitukuko m'msikamu. Bola tisiye kupereka ndalamazo ndipo tilembe galimoto yathu kuchotsa nyasizi," adatero Jalisi.

Mbali ya khonsolo, mkulu wa bungweli a Archangel Bakolo komanso Mfumu ya mzindawu a Christopher Jana, avomereza kuti vuto lilipo. Iwo ati ena mwa magalimoto omwe amachotsa zinyalala aonongeka ndipo pakali pano akudikira kuti akonzedwe.

"Koma izi sizikutanthauza kuti sitikupeza njira. Panopa tapeza kampani yomwe ikugwira ntchito yochotsa zinyalalazi pakadali pano, pomwe tikukonza magalimoto athu ena," atero a Jana.

Zikuwoneka kuti nthawi yofuna kusintha yakwana. Amalonda akufuna khonsolo ichite zambiri kuposa kungolandira ndalama. Ndipo ngati zinthu sizisintha, mwina adzatenga zinthu m'manja mwawo mwachitsanzo, kulemba galimoto yawo yochotsa zinyalala.

Kodi izi zikusonyeza kusasamala kwa mabungwe a boma? Kapena ndi kusowa kwa zinthu zofunikira monga magalimoto? Chifukwa chilichonse chili choncho, amalonda a Chinamwali sakufuna kukhala chete. Tsopano ndi nthawi yoti mphamvu ya amalonda imveke.

Comments

Popular posts from this blog

Mfumu Yaikulu Gawa Undi Aletsa Magule Opanda Ulemu pa Kulamba 2025

Ngozi ya Sitima ya M'madzi ku Likoma: Atatu afa, ena asanu ndi atatu apulumutsidwa

Nkhani Yachisoni ku Mchinji: Bambo wamangidwa Atapha Mwana Wake Chifukwa Chosamvera