Dziko Lonse Likulira: Papa Francis Wamwalira
Dzulo ku Makoka Research Farm, yomwe kale inkatchedwa Makoka Research Station, ku Zomba kunachitika chionetsero chachikulu cha ulimi. Pa mwambowu, alimi anauzidwa kuti nthawi yakwana yoti asiye kulima mwachizolowezi ndipo ayambe kugwiritsa ntchito njira zamakono, makamaka kulima mbeu zopilira ku ng'amba.
![]() |
| Alimi aku Zomba |
A Jessie Mvula, Wogwira Ntchito ku Makoka Research Farm, anati mbeu monga mbatata, nthochi, mapira, soya, komanso chimanga cha makono zikhoza kubweretsa zokolola zambiri ngati alimi atatsatira malangizo a ulimi moyenera. Iye anafotokoza kuti limodzi mwa zolinga zawo ndi kulumikiza alimi ndi makampani kuti azitha kugulitsa zokolola zawo pa mitengo yabwino. Izi zingathandize alimi kukhala ndi chakudya chokwanira komanso ndalama m'matumba mwawo.
![]() |
| Jessie Mvula |
A Mvula anawonjezera kuti:
“Tili okonzeka kumalumikizitsa alimi ndi makampani kuti azikagulitsa zokolola zawo kumeneko pa mitengo yabwino.”
Bungwe la Center for Agricultural Transformation (CAT) lomwe lidatsogolera chionetserocho, kudzera mwa mkulu wake a McLeod Nkhoma, linatsindika kuti alimi sayenera kungodalira kulima kokha, koma azigwiritsa ntchito njira zamakono monga ulimi wa nthilira komanso kugwiritsa ntchito matekinoloje ena a luso.
Nyakwawa Ndechere, pansi pa Senior Chief Mlumbe, adati kudzera m'misonkhano yomwe akhala akuchititsa, akulimbikitsa anthu awo kuti asiye njira zakale zosabala bwino, ndipo atembenuke mtima kulimbikira ulimi wamakono womwe uli ndi phindu lalikulu.
Zimene Tinga Phunzire:
1. Kulima mbeu zopilira ku ng’amba kuli ndi phindu lalikulu.
2. Kugwiritsa ntchito njira zamakono monga ulimi wa nthilira kumakulitsa zokolola.
3. Alimi ayenera kulumikizana ndi makampani kuti apeze misika yabwino.
4. Bungwe la CAT likugwira ntchito yolimbikitsa chisinthe cha njira za ulimi.
Nthawi yakwana yoti ulimi ukhale gwero la chuma chenicheni. Tiyeni tichite kusintha!
Comments
Post a Comment