Dziko Lonse Likulira: Papa Francis Wamwalira

Image
Lero dziko lonse likulirira. Mtumiki wathu, mtumwi wa mtendere, mtsogoleri wa Tchalitchi cha Katolika Papa Francis   wamwalira ali ndi zaka 88 . Nkhaniyi yatsimikizidwa ndi Vatican m'mawa uno, ndipo ikufalikira mofulumira padziko lonse lapansi. Papa Francis  Papa Francis, anabadwa ngati Jorge Mario Bergoglio ku Argentina, anali Papa woyamba kuchokera ku America, komanso wa mtundu wa Jesuit. Kuyambira atasankhidwa mu March 2013 , anasankha dzina Francis osati chifukwa chokopa, koma kuti akhale ngati Mtumiki wa osauka St. Francis of Assisi . Sanali Papa wa mphamvu anali Papa wa mtima . Anakana kukhala m'nyumba zokongola za Vatican, ndipo anasankha kukhala m'chipinda chaching'ono chisonyezo cha moyo wake wopanda kudzikuza. Papa Francis anali wolimba mtima. Anayankhula za kusintha kwa nyengo (climate change), kusasiyana kwa olemera ndi osauka, kulandira othawa kwawo, komanso za chikondi cha Mulungu kwa aliyense – ngakhale amene ena amawawona ngati osayenera. Anati: “...

Mlandu wa Alfred Gangata Uchedwa pa Zifukwa za Kulemba Mwachinyengo


Pa bwalo la milandu la Magistrate, lero kwachitika zachilendo pomwe mlandu wa a Alfred Gangata, wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipani cha DPP ku Central Region, wachititsa chisokonezo. 

Alfred Gangata ndi anthu ena

Izi zachitika chifukwa oweruza a Austin Banda alamula kuti a mbali ya boma akalembenso bwinobwino mfundo za mlanduwo (zomwe zimadziwika kuti "particulars of the offence") chifukwa sizinasonyeze bwino kuti a Gangata akuwazenga mlandu wanji.

A Gangata akuwaganizira kuti anapeza satifiketi ya fomu folo mwachinyengo, ndipo pakadali pano ali pa belo ndipo lero anapita kubwalo la milandu kuti akavomere kapena kuukana mlanduwu. Koma ndondomekoyi sinatheke chifukwa a mbali yoyankhapo mlandu anabweretsa mtsutso wokhudza mmene mfundo za mlanduwo zalembedwera.

Oimira boma, a Charles Panyani, anatsutsana ndi zimenezi, akutsindika kuti mfundo za mlanduwo zalembedwa bwinobwino. Komabe, oweruza a Banda sanavomereze izi, ndipo analamula kuti mlanduwo ulembedwe kuchokera poyambiranso, ndi kufotokoza bwinobwino zolakwa zomwe akuwaganizira a Gangata.

Lamulo ili likutanthauza kuti mlandu wa a Gangata wachoka pa siteji yomwe ankayembekezera kuti athane nawo mwachindunji, ndipo tsopano akuyembekezera kuti boma libweretse milandu yomwe ili yomveka komanso yolemekezeka molingana ndi malamulo.

Zikuwonekeratu kuti milandu ikafika ku bwalo, si nkhani yokungoyambitsa basi, koma lemba lililonse, ndime iliyonse, komanso tanthauzo lake zimakhala zofunika kwambiri.

Tiyeni tiwone momwe nkhaniyi iyendere m’masiku akubwerawa.

Comments

Popular posts from this blog