Dziko Lonse Likulira: Papa Francis Wamwalira
Msika wa fodya ku Limbe wayimitsidwa kwakanthawi pambuyo poti alimi ambiri adadzudzula mtengo wotsika wa fodya, womwe ukufika pa $1.15 pa kilo. Alimi ati mtengo uwu ndi wopweteka chifukwa sufanana ndi ndalama zomwe adagwiritsa ntchito polima fodya kuchokera ku munda.
![]() |
| Msika wafodya wa Limbe |
Alimi ambiri amati ntchito yawo ya chaka chonse, kuphatikiza ndalama zogulira feteleza, mankhwala, ndi ntchito yolima, sizikuoneka ngati zikulipidwa moyenera ndi mtengo umene akupezawu. "Tikuvutika kwambiri. Tilimi tikuyika ndalama zambiri komanso nthawi yochuluka mu ulimiwu, koma pamapeto pake sitikupeza chilungamo," anatero mlimi wina m’modzi amene timacheza naye.
Mandala, itapita ku msika wa Limbe, idapeza kuti mtengo wokwera kwambiri wa fodya wogulitsidwa mpaka pano wafika pa $3.20 pa kilo. Komabe, izi zikuoneka ngati zikusiyana kwambiri ndi mtengo wamba wa $1.15, zomwe zikuchititsa kuti alimi ambiri asakhutitsidwe.
Zikuoneka kuti pali kusiyana kwakukulu pakati pa zomwe alimi akuyembekezera ndi zomwe msika ukupereka. Pofuna kupewa mavuto ena, oyang’anira msika wa Limbe adaganiza zoimitsa malonda kwakanthawi kuti akambirane ndi anthu okhudzidwa.
Nthawi ikuwonetsa kuti pofuna kukulitsa chuma cha mlimi, pali kufunika kokonza momwe fodya amagulitsidwira komanso kuwonetsetsa kuti alimi akulandira mtengo woyenerera ndi wolingana ndi ntchito yawo.
Tiyeni tipitirize kutsatira nkhaniyi kuti tidziwe zomwe zidzachitike mtsogolo pa msika wa fodya ku Limbe.
#Fodya #LimbeMarket #UlimiWoyenerera #MalondaAmisika
Comments
Post a Comment