Dziko Lonse Likulira: Papa Francis Wamwalira
M’dera la Naming’azi mu Zomba Malosa Constituency, anthu akulira ndi maliro a khansala wakale Willy M’manga yemwe anali membala wa chipani cha Democratic Progressive Party (DPP). A M’manga amwalira posachedwapa pa Chipatala Chachikulu cha Zomba, komwe amalandira chithandizo cha matenda a shuga.
![]() |
| Willy M'manga |
Willy M’manga anali munthu wodziwika komanso wolemekezeka m’dziko lake, ndipo anatumikira bwino anthu a m’dera la Naming’azi pa nthawi yomwe anali khansala.
Malinga ndi wapampando wa khonsolo ya Zomba, Khansala Brazio Chinthenga, thupi la khansala M’manga liyikidwa mmanda mawa, Lamlungu, m’dera la kwawo ku Naming’azi. A Chinthenga atsimikiza za imfayi ndipo ati banja limodzi ndi khonsolo apereka zambiri zokhudza dongosolo la maliro.
Pamene anthu a ku Naming’azi akukonzekera kumupereka kwa ambuye khansala wakale, ambiri akukumbukira ntchito yake yabwino komanso chikondi chimene anali nacho pa dera lake. Pumulani mumtendere a Willy M’manga.
Comments
Post a Comment