Dziko Lonse Likulira: Papa Francis Wamwalira

Image
Lero dziko lonse likulirira. Mtumiki wathu, mtumwi wa mtendere, mtsogoleri wa Tchalitchi cha Katolika Papa Francis   wamwalira ali ndi zaka 88 . Nkhaniyi yatsimikizidwa ndi Vatican m'mawa uno, ndipo ikufalikira mofulumira padziko lonse lapansi. Papa Francis  Papa Francis, anabadwa ngati Jorge Mario Bergoglio ku Argentina, anali Papa woyamba kuchokera ku America, komanso wa mtundu wa Jesuit. Kuyambira atasankhidwa mu March 2013 , anasankha dzina Francis osati chifukwa chokopa, koma kuti akhale ngati Mtumiki wa osauka St. Francis of Assisi . Sanali Papa wa mphamvu anali Papa wa mtima . Anakana kukhala m'nyumba zokongola za Vatican, ndipo anasankha kukhala m'chipinda chaching'ono chisonyezo cha moyo wake wopanda kudzikuza. Papa Francis anali wolimba mtima. Anayankhula za kusintha kwa nyengo (climate change), kusasiyana kwa olemera ndi osauka, kulandira othawa kwawo, komanso za chikondi cha Mulungu kwa aliyense – ngakhale amene ena amawawona ngati osayenera. Anati: “...

Agamulidwa Zaka 9 chifukwa chogwirira mwana wake

 Elisa Balakasi, mwamuna wa zaka 40, wagamulidwa zaka 9 kundende chifukwa chogwiririra mwana wake wamkazi wazaka 14 yobadwa.

Elisa Balakasi

A Balakasi adagonana ndi mwana wawo mu mwezi wa February, pomwe Balakasi ananyengerera mwanayi ndi ndalama zokwana K5000 asanachite naye zadamazi patchire pafupi ndi nyumba yawo. Nkhaniyi inatuluka mwezi wa March, mwana atayamba kuonetsa zizindikiro zoti ali ndi pakati. Amayi ake atafunsa, mwanayo adawulula zowawa zomwe zinamuchitikira, ndipo nkhaniyi inaperekedwa ku polisi ya Namizana.

Woimira boma pa mlandu, a Thokozani Moloko, adalongosola nkhaniyi m'bwalo la milandu la ku Mchinji, ndipo mneneri wa polisi a Limbani Mpinganjira adatsimikiziranso nkhaniyi kwa anthu.

Ataima m’bwalo la milandu, Balakasi adapempha kulandira chilango chochepa ponena kuti mavuto a m’banja ndi amene adamukakamiza kuchita zimenezo. Koma oweruza a Juma Chilowetsa sanamvepo kanthu ka chisoni. Iwo anati, “Mlandu ngati uwu wachuluka kwambiri m’dziko muno, ndi chifukwa chake chilango chiyenera kukhala chokhwima.”

Balakasi amachokera ku mudzi mwa Nyakwawa, m’dera la mfumu yayikulu Mavwere ku Mchinji.


Comments

Popular posts from this blog

Mfumu Yaikulu Gawa Undi Aletsa Magule Opanda Ulemu pa Kulamba 2025

Ngozi ya Sitima ya M'madzi ku Likoma: Atatu afa, ena asanu ndi atatu apulumutsidwa

Nkhani Yachisoni ku Mchinji: Bambo wamangidwa Atapha Mwana Wake Chifukwa Chosamvera