Dziko Lonse Likulira: Papa Francis Wamwalira

Image
Lero dziko lonse likulirira. Mtumiki wathu, mtumwi wa mtendere, mtsogoleri wa Tchalitchi cha Katolika Papa Francis   wamwalira ali ndi zaka 88 . Nkhaniyi yatsimikizidwa ndi Vatican m'mawa uno, ndipo ikufalikira mofulumira padziko lonse lapansi. Papa Francis  Papa Francis, anabadwa ngati Jorge Mario Bergoglio ku Argentina, anali Papa woyamba kuchokera ku America, komanso wa mtundu wa Jesuit. Kuyambira atasankhidwa mu March 2013 , anasankha dzina Francis osati chifukwa chokopa, koma kuti akhale ngati Mtumiki wa osauka St. Francis of Assisi . Sanali Papa wa mphamvu anali Papa wa mtima . Anakana kukhala m'nyumba zokongola za Vatican, ndipo anasankha kukhala m'chipinda chaching'ono chisonyezo cha moyo wake wopanda kudzikuza. Papa Francis anali wolimba mtima. Anayankhula za kusintha kwa nyengo (climate change), kusasiyana kwa olemera ndi osauka, kulandira othawa kwawo, komanso za chikondi cha Mulungu kwa aliyense – ngakhale amene ena amawawona ngati osayenera. Anati: “...

A bambo awiri awanjata ku Thyolo chifukwa chogulisa chimanga Cha boma

Thyolo, dziko lathu lokoma lino, silimalephera kutipatsa nkhani zomwe zingakupangitseni kuseka ngakhale mutavutika ndi njala yomwe chimanga chachitiridwachi. Lero tili ndi nkhani yomwe ikungofunika chinthu chimodzi chokha: popcorn, chifukwa iyi ndi drama ya "matumba 10 a chimanga" yomwe ingapose ngakhale series ya Money Heist!

Kodi zachitika bwanji?

Chinachitika n’choti boma linali pa mission yabwino—kupereka chimanga kwa anthu omwe akuvutika ndi njala ku Ntambanyama, m’boma la Thyolo. Galimoto yodzaza ndi matumba 700 a chimanga inanyamuka ngati momwe zimayendera nthawi zambiri... koma apa, zinthu zinapota ngati sitiroko yatsopano ya WhatsApp.

M’galimoto munali dalaivala, mulonda wa khonsolo dzina lake Aubrey Malindi, ndi munthu wina wotchedwa Leonard Jika, wazaka 39, yemwe amagwira ntchito ngati wothandizira wa dalaivalayo. Tsono anthu awa m'malo moti azingopereka chimangacho monga momwe zinalili pa plan, anaganiza zochita business yosadziwika m’malemba a khonsolo. Yes! Private sector at its worst!

Iwo ananyamuka ndi chimanga chonse kupita ku Ntambanyama, koma apa ndiye amakhala ngati aikuletsa GPS. Kufika pa msewu, analowetsa mode ya “business unusual”, ndi kuyamba kugulitsa matumba khumi a chimanga kwa mavenda m’mbali mwa msewu—ngati ali pa pulogalamu ya Buy One, Feed None.

Koma anthu sanangoyang’ana chabe.

Zinthu zinali ngati filimu. Anthu akaona chimanga cha boma chikugulitsidwa m'manja mwa vendors, anayamba kuchita investigation mode. Zotsatira zake? Azibambo athuwo anathawa galimoto ngati ikulipuka – kuisiyira pakati pa msewu, pofuna kuti apulumuke ndi miyoyo yawo. Komabe sizinatheke. Apolisi a Thyolo anachita mwachangu—kugwira a Malindi ndi a Jika ngati mchenga wa pa nyanja.

Dalaivala? Watha ngati bowa m’nkhalango.

Apa ndiye nkhani yasintha! Ngakhale chimanga cha matumba 10 chatayika, malipoti a khonsolo akuti chimanga chonse – 700 bags – sichinasowe. Eya, boma lakana kulandira loss report. Matumbawo ndi okwanira. Nanga 10 aja? Mwina anali sample packs kapena "promo packs" monga momwe amakonda kunena m'masitolo akulu akulu.

Chondiphunzitsa ife apa n’chakuti:

Ngati mukugwira ntchito yosamalira chimanga cha boma, musayese kuchita short-cut yopita ku Ntambanyama kudzera m’misewu ya vending business. Boma liri ndi maso, anthu ali ndi makutu, ndipo apolisi ali ndi ma handcuffs omwe sali pa budget koma amapezeka nthawi zonse.

Tidzawona momwe nkhaniyi itathere, koma kwa pano, tikungoti: ndalama zatha, chimanga chapita, koma drama ndiye yatsala!

Siyani maganizo Anu Kuma comment 

Comments

Popular posts from this blog

Mfumu Yaikulu Gawa Undi Aletsa Magule Opanda Ulemu pa Kulamba 2025

Ngozi ya Sitima ya M'madzi ku Likoma: Atatu afa, ena asanu ndi atatu apulumutsidwa

Nkhani Yachisoni ku Mchinji: Bambo wamangidwa Atapha Mwana Wake Chifukwa Chosamvera